Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Amangidwa kaamba koganiziridwa kuti adagwilirira mwana

Apolisi mu mzinda wa Zomba amanga a Andrew Banda a zaka 25 zakubadwa powaganizira kuti anagwirira mwana wazaka 12.

Ofalitsankhani wa Polisi ya Zomba, a Patricia Sipiliano, ati a Banda anamutenga mwanayo pa msika wina pamene iye amagulitsa zigege ndipo anapita naye ku malo ena ogona alendo komwe adakapalamula mlanduwo.

Anthu ena atawona izi adatsina khutu makolo a mwanayo, omwe anathamangira ku katula nkhaniyi ku Polisi.

A Banda akawonekera ku bwalo la milandu komwe akayankhe mlandu ogwililira.

Iwo amachokera m’mudzi wa Majanga kwa Mfumu yayikulu Kachenga m’boma la Balaka.

#MBCDigital
#Manthu

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

GOOD PROGRESS IN RESTORING PUBLIC SERVICE DELIVERY – CHAKWERA

Secret Segula

Silver Strikers FC at the helm of TNM Super League

AMBASSADOR YOUNG RETIRES

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.