Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Amangidwa kaamba koganiziridwa kuti adagwilirira mwana

Apolisi mu mzinda wa Zomba amanga a Andrew Banda a zaka 25 zakubadwa powaganizira kuti anagwirira mwana wazaka 12.

Ofalitsankhani wa Polisi ya Zomba, a Patricia Sipiliano, ati a Banda anamutenga mwanayo pa msika wina pamene iye amagulitsa zigege ndipo anapita naye ku malo ena ogona alendo komwe adakapalamula mlanduwo.

Anthu ena atawona izi adatsina khutu makolo a mwanayo, omwe anathamangira ku katula nkhaniyi ku Polisi.

A Banda akawonekera ku bwalo la milandu komwe akayankhe mlandu ogwililira.

Iwo amachokera m’mudzi wa Majanga kwa Mfumu yayikulu Kachenga m’boma la Balaka.

#MBCDigital
#Manthu

Related posts

Gestational Diabetes likely among expectant mothers, study reveals

Romeo Umali

Mayi akagwira ukayidi kwa zaka ziwiri atavulaza mamuna wake

Romeo Umali

Local chiefs, subordinates nabbed over chieftaincy wrangles

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.