Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Oganiziridwa kufalitsa nkhani zabodza akhalabe mchitokosi

Bwalo la milandu la Magistrate munzinda wa Lilongwe lati lipitiriza kumva mulandu wa oganiziridwa kuti amafalitsa nkhani zabodza kudzera pa intaneti a Chiyanjano Mbedza, Lachiwiri pa 30 July 2024.

Bwaloli lati a Chiyanjano Mbedza akhalabe mchitokosi kufikira Lachiwiri nthawi ya 2 koloko masana polola oyimira boma pa milandu kumalizitsa ntchito yofufuza yomwe yangotsala yochepa.

A Mbedza akuwaganizira kuti pa 25 June 2024 anafalitsa uthenga wabodza pa intaneti okhudza imfa ya malemu Dr Saulos Chilima.

Powerenga chikalata cha chigamulochi mmalo mwa oweruza, a Rhodrick Michongwe, a Benaderta Kalua anati izi ndizotsutsana ndi gawo 60 la malamulo aakulu oyendetsera dziko lino.

Olemba ndikujambula: Emmanuel Chikonso ndi Thokozani Jumpha.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Bande apempha mafumu atsogolere chitukuko

Blessings Kanache

Save The Children yapereka mbaula zamakono ku Lilongwe

Lonjezo Msodoka

‘Mavuto simathero a moyo’

Paul Mlowoka
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.