Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Oganiziridwa kufalitsa nkhani zabodza akhalabe mchitokosi

Bwalo la milandu la Magistrate munzinda wa Lilongwe lati lipitiriza kumva mulandu wa oganiziridwa kuti amafalitsa nkhani zabodza kudzera pa intaneti a Chiyanjano Mbedza, Lachiwiri pa 30 July 2024.

Bwaloli lati a Chiyanjano Mbedza akhalabe mchitokosi kufikira Lachiwiri nthawi ya 2 koloko masana polola oyimira boma pa milandu kumalizitsa ntchito yofufuza yomwe yangotsala yochepa.

A Mbedza akuwaganizira kuti pa 25 June 2024 anafalitsa uthenga wabodza pa intaneti okhudza imfa ya malemu Dr Saulos Chilima.

Powerenga chikalata cha chigamulochi mmalo mwa oweruza, a Rhodrick Michongwe, a Benaderta Kalua anati izi ndizotsutsana ndi gawo 60 la malamulo aakulu oyendetsera dziko lino.

Olemba ndikujambula: Emmanuel Chikonso ndi Thokozani Jumpha.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Ana a m’mudzi bwerani muthandize kwanu – Mfumu Mwamulowe yatero

MBC Online

Dr Chakwera akhudzika ndi imfa ya bambo Boucher Chisale

Simeon Boyce

Mpikisano wa 1 NICO Netball watentha

Foster Maulidi
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.