Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Nzika yaku Mozambique ayigwira itathyola ndikuba mnyumba

Apolisi m’chigawo chakummwera amanga Richard Herema  wazaka 42, yemwe kwawo ndi ku Mozambique, pomuganizira kuti iyeyo pamodzi ndi amzake,l anathyola nyumba ziwiri ndikuba ndalama zoposa K3 million komanso foni zam’manja kudera la Thornwood ku Mulanje.

Ofalitsankhani wapolisi ku Mulanje, Innocent Moses, wati Herema anali mgulu la mbava 40 zomwe zakhala zikuvutitsa mderalo.

Pakadali pano, apolisi akufufuza amzake a Herema omwe anathawa.

Herema amachokera mmudzi wa Mbizi, Mfumu yaikulu Nazombe ku Milanje m’dziko la Mozambique koma amakonza njinga zakapalasa zowonongeka kuno ku Malawi.

#MBCDigital
#Manthu

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

PARLIAMENT ADOPTS A REPORT TO HAVE A FIXED HOUSING RATE FOR RETIRED CHIEF JUSTICES

MBC Online

Senior Chief Kapoloma dies

MBC Online

CEPA PROMOTES ORGANIC SOIL MANAGEMENT

Natasha Muthete
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.