Mtsogoleri wa chipani chatsopano cha People’s Development (PDP), Kondwani Nankhumwa, wati chipanichi chabwera kudzasintha Malawi kukhala dziko lodzidalira pa chakudya, la umodzi ndinso kulimbikira pantchito.
Poyankhula pamsonkhano wa atolankhani mumzinda wa Blantyre, iwo ati chipanichi chithetsa m’chitidwe okakamira m’maudindo muzipani.
A Nankhumwa atinso a Malawi akufunika chipani chomwe chingamalore anthu kupikisana momasuka.
Wolemba: Blessings Cheleuka