Malawi Broadcasting Corporation
Crime Development Local News Nkhani

Mlandu wa Bushiri wayima kaye!

Bwalo lamilandu la Chief Resident Magistrate ku Lilongwe layamba laima kaye kumva mulandu omwe boma la South likufuna kuti Banja la a Bushiri lipite mdzikolo kukayankha milandu yomwe anawatsegulira kufikira pa 17 July Chaka chino.

Bwaloli laimitsa mlanduwu chifukwa mkulu oyimira boma komanso yemwe akutsogolera mlanduwu, a Dzikondianthu Malunda, akuti akudwala.

Mmodzi mwa oimira banja la a Bushiri, a Annelene Van De Heever, anati mbali yawo ndiyokonzeka kupitiriza kufunsa mboni yaboma zokhudza mlanduwu.

Bwalo lamilanduli linayamba kumvanso mlanduwu lachitatu sabata ino atauimitsa mu March chaka chino kuti mbali yoimira ozengedwa ikonzekere mokwanira.

 

Related posts

Chimwendo to vye for MCP Secretary General position

Mayeso Chikhadzula

NICE facilitates civic engagement in Dedza

Romeo Umali

MoH proposes mandatory use of ID, birth certificates in accessing health services

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.