Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Tipitiriza kuthandiza – NBS Bank

Bank ya NBS yathandiza anthu okalamba komanso a ulumali ndi matumba a ufa wa chimanga kummwera kwa boma la Chiradzulu.

Poyankhula popereka thandizoli, mkulu wa Branch ya Limbe, a Twaibu Nnani, ati bankiyi ipitiriza kuthandiza osowa kudzera mu njira zosiyanasiyana.

Ndipo mfumu yaikulu Mpunga yapempha mabungwe akufuna kwabwino kuti athandize mabanja omwe akhudzidwa ndi njala.

Malinga ndi a Mpunga thandizoli ati ndi lapafupifupi K3.5 million.

Wolemba: Blessings Cheleuka

 

Related posts

Temwa aveka makanda pa chipatala cha Kamuzu Central

Romeo Umali

Nyimboyi ithandize onse osweka mitima – Sife Mw

Romeo Umali

‘Chisankho chayenda bwino’

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.