Malawi Broadcasting Corporation
Development Local News Nkhani

Khonsolo ya mzinda wa Lilongwe yagumula sitolo zoposa 60 mkatikati mwa Lilongwe

Khonsolo ya mzinda wa Lilongwe m’mbandakucha walero wagwetsa ndi kugumula nyumba zoposa 60 zogulitsira katundu ntauni ya munzinda wa Lilongwe kamba koti eni ake anazimanga mosatsata malamulo.

izi zikudza pomwe unduna wazamalo posachedwapa walengeza zoyamba ntchito yogwetsa nyumba zomwe zamangidwa mosatsata mapulani.

Arfoso Zudu Jamali, m’modzi wa eni nyumba azigumulazo, adandaula ponena kuti chenjezo linali la masiku 29 ndipo agumula masikuwa asanakwane.

A Jamali ati mashopu osankhika ndi omwe awagumula kusiya ena omwe akuti ndi anzika za maiko ena.

Wachiwiri kwa wapampando wa eni ma minibus, a Heirman Msowoya, ati iwo avomereza zomwe undunawu wachita kaamba koti anawapatsa chenjezo asanayambe ntchito yomanga pamalopo.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

UNDP offers advice to foster SME growth in Malawi

Salomy Kandidziwa

CHAKWERA TO ATTEND INAUGURATION OF UPGRADED NACALA PORT

McDonald Chiwayula

MBC seeks improved partnership with community radios

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.