Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Sports Sports

Mtsogoleri wa FIFA akapepesa maliro a Dr Chilima

Mtsogoleri wa bungwe loyang’anira masewero a mpira wa miyendo padziko lonse la pansi la FIFA, a Gianni Infantino, akuyembekezeka kupepesa mwapadera ku banja la malemu Dr Saulos Chilima amene anali wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino.

Iwo akapepesanso kwa mtsogoleri wa dziko lino, Dr Lazarus Chakwera.

A Infantino afika m’dziko muno lachiwiri madzulo kudzera pa bwalo la ndege la Kamuzu mu mzinda wa Lilongwe pamene analandiridwa ndi mtsogoleri oyendetsa masewero a mpira wa miyendo m’dziko muno, a Fleetwood Haiya.

Koma a Infantino ayimitsa kaye dongosolo limene anakonza kuti ayambepo ntchito yoyendera masewero a mpira wa miyendo kaamba ka chisoni chomwe chakuta dziko la Malawi.

 

 

Related posts

Over 18,000 farmers redeem SAPP II RED farm inputs ‎

MBC Online

‘Tisalore katangale pa ntchito zaumoyo’

Romeo Umali

BUSHIRI REACHES OUT TO FOOD INSECURE FAMILIES IN LL RURAL

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.