Malawi Broadcasting Corporation
Culture Development Local Local News Nkhani

Mafumu ayamikira ndondomeko yolembetsa malo

Mafumu a m’boma la Blantyre ayamikira boma pokhazikitsa ntchito yolembetsa umwini wa malo.

Mfumu yayikulu Kunthembwe inati ntchito yolembetsa maloyi ndi yabwino kwambiri kaamba kakuti ichepetsa ziwawa zimene zimabwera chifukwa cha kusamvana pa nkhani zokhudza malo.

Iwo amayankhula izi pa msonkhano wapakati pa unduna wa zamalo ndi mafumu okhala m’mbali mwa mtsinje wa Shire.

Mkulu oona za zantchito kuunduna wa zamalo, a Dr Victor Sandikomda, anati mafumu ndi ofunika kuti amvetse bwino malamulo atsopano a malo chifukwa iwo ndi eni nthaka.

Ntchitoyi ikutheka ndi thandizo lochokera ku bungwe la Malawi Watershed Services Improvement Project.

Related posts

ESCOM builds 29 modern houses for Neno and Mwanza communities

Romeo Umali

No time to celebrate –– Kumilambe

Romeo Umali

Chipatala cha South Lunzu chikupempha thandizo

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.