Malawi Broadcasting Corporation
Entertainment Entertainment Local Local News Nkhani

Mikozi ibweranso, eni ake atero

Mwini watsamba la mchezo la Mikozi, a Bright ‘Excess’ Chiligo, watsutsa mphekesera zimene zikumveka kuti tsamba lake anthu alichita chiwembu kuti lisowe pa makina a internet.

Chiligo wati tsambali libweleranso Lachisanu chifukwa pali ntchito imene akugwira yopanga tsambali kukhala lotetezeka kwa anthu achinyengo.

“Tawona kuti pa internet pachuluka masamba a mchezo amene akubera dzina lathu la Mikozi ndipo akumayika zinthu zoyipa,” iye anatero.

Anawonjezeranso kuti zimenezi zapangitsa kuti azilandira madandaulo ochuluka kuchokera kwa anthu.

 

Related posts

Air Cargo Malawi to use MDF aircraft for cargo transportation

Rabson Kondowe

MRA seeks solutions to alleviate congestion, revenue loss

MBC Online

NGORA records 54% compliance rate

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.