Malawi Broadcasting Corporation
Entertainment Entertainment Local Music News Nkhani

Malinga Mafia wapepesa atachedwa ku Illusionz

Katswiri oyimba Dancehall, Malinga Mafia, wapepesa kwa okonda nyimbo zake kaamba kokanika kuyimba ku phwando lamayimbidwe la Illusionz lomwe likuchitikira pagombe m’boma la Mangochi.

Katswiriyu amayenera kutsekulira phwandoli Lachisanu madzulo, koma m’malo mwake, ma Blacks ndi amene anagwira ntchitoyi.

Malinga anachedwa ndi ola limodzi chifukwa iye pamodzi ndi oyimba ena anagwiritsa ntchito khomo lolowera gulu kuphwandoli.

“Zachitikazi likhale phunziro kwa omwenso akonza mwambowu, adzisiyanitsa khomo lolowera anthu odzayimba ndi odzaonelera kuti padzikhala dongosolo,” Malinga anatero.

Phwandoli ndi la masiku atatu. Oyimba akunja monga Eemoh ndi Dj Tira afika kale ndipo Dj Maphorisa ndi Kabza akuyembekezeka kuti afike lero.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

NBM donates K2 million to support Business Journalists’ AGM

Arthur Chokhotho

Philanthropist hails Lions Club

Alinafe Mlamba

CHAKWERA LAUNCHES 2022 AIP

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.