Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Bambo alamulidwa agwire jere kwa zaka 12 atagwilira

Bwalo la milandu la First Grade m’boma la Mzimba lalamula a Emmanuel Khowaya,32, kuti akagwire ukayidi wa kalavula gaga kwa zaka khumi ndi ziwiri atawapeza olakwa pa mlandu ogwilira mwana wazaka zisanu ndi zitatu.

A Khowaya adapalamula mlanduwu mu shopu yawo imene amayikitsa nyimbo komanso ku tchaja lamya za m’manja.

M’bwalo la milandu, a Khowaya anavomereza kuti ndi olakwa koma anapempha kuti awavere chisoni chifukwa alibe makolo komanso amayang’anira achemwali awo awiri ndi agogo awo.

Koma First Grade Magistrate sanamvere izi ndipo anawagamula kuti apite kundende chifukwa anaphwanya lamulo lomwe lili pa ndime 138.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

TISADULE MITENGO MWACHISAWAWA

MBC Online

Chakwera to preside over Cyclone Freddy Memorial Service

Romeo Umali

10 feared dead in Thyolo accident

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.