Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Bambo alamulidwa agwire jere kwa zaka 12 atagwilira

Bwalo la milandu la First Grade m’boma la Mzimba lalamula a Emmanuel Khowaya,32, kuti akagwire ukayidi wa kalavula gaga kwa zaka khumi ndi ziwiri atawapeza olakwa pa mlandu ogwilira mwana wazaka zisanu ndi zitatu.

A Khowaya adapalamula mlanduwu mu shopu yawo imene amayikitsa nyimbo komanso ku tchaja lamya za m’manja.

M’bwalo la milandu, a Khowaya anavomereza kuti ndi olakwa koma anapempha kuti awavere chisoni chifukwa alibe makolo komanso amayang’anira achemwali awo awiri ndi agogo awo.

Koma First Grade Magistrate sanamvere izi ndipo anawagamula kuti apite kundende chifukwa anaphwanya lamulo lomwe lili pa ndime 138.

 

Related posts

Chakwera leaves USA for Malawi

Mayeso Chikhadzula

PRISAM TO LAUNCH SACCO FOR PRIVATE SCHOOLS

MBC Online

Phyzix set to invade Mzuzu

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.