Malawi Broadcasting Corporation
Education Entertainment Entertainment Local Local News Nkhani

‘Kanema wa Belinda alimbikitsa atsikana’

Amene anajambula kanema wa Belinda, gulu la Remnant Lions, ati ali ndi chikhulupiliro kuti kanemayu alimbikitsa atsikana kuti asamafooke pa maphunziro ngakhale atakumana ndi mavuto, kuphatikizapo kutenga pakati.

Otsogolera ntchito yojambula m’kanemayu, a Tionge Chisiza, ati aonetsetsa kuti seweroli lifikire aliyense, makamaka m’sukulu zakumudzi.

Iwo amayankhula izi Lachisanu madzulo atawonetsa kanemayu mu nzinda wa Lilongwe.

“Tikufuna aliyense yemwe ali ndi chidwi cholimbikitsa maphunziro aonere kanemayi,” a Chisiza anatero.

Kanemayu anamuonetsa kale munzinda wa Blantyre ndipo pali chikonzero kuti akamuonetsenso ku Mzuzu ndi ma boma ena.

Gulu la Remnant Lions analitsogolerako ndi malemu a Thlupego Chisiza.

 

Related posts

14 to benefit from Mpinganjira’s business capital project

Rabson Kondowe

Malawi International Arbitration Centre gets financial boost

Rabson Kondowe

Institutions providing poor quality food to children — Committee

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.