Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani

Zokonzekera msonkhano wapachaka wa Surveyors Institute of Malawi zili mchimake

Bungwe la Surveyors Institute of Malawi lati chilichonse chili mchimake pa zokonzekera za msonkhano wawo waukulu wapachaka umene uyambe pa 26 mpakana pa 27 mwezi uno.

Mlembi wamkulu wa bungweli, a Bernard Mleta, ndi amene amayankhula izi Lachiwiri masana atalandira thandizo la ndalama zokwana K3 million kuchokera ku kampani ya Property Solutions Limited.

A Mleta anayamikira kampaniyi kaamba ka thandizoli chifukwa laonetsa poyera kuti ali ndi chidwi chokweza ntchito zabungweli.

Mkulu wa Property Solutions, a Willy Mwawa, anati athandiza chifukwa akudziwa zakufunika kwa mwambowu komanso ngati membala wa bungweli, ndi udindo wawo kutero.

Kampaniyi imagwira ntchito younika kuchuluka ndi mlingo wa zinthu kapena malo m’dziko muno.

 

Related posts

Female MSCE top performers to be awarded

Romeo Umali

PRESIDENT CHAKWERA COMMISSIONS POLICE STAFF HOUSES

MBC Online

Malawi International Arbitration Centre to launch operations by early September

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.