Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Walipira chindapusa chifukwa chonyoza wodwala AIDS

Khoti lina ku Balaka lalamula bambo wazaka 45, Frank Nazombe, kuti apereke chindapusa cha ndalama zokwana K65,000 chifukwa chonyoza mayi wodwala matenda a AIDS.

Mneneri wapolisi ku Balaka, a Gladson M’bumpha, wati Nazombe anayambana ndi mayiyo ku mowa.

Tsiku lotsatira, Nazombe analawira mammawa kupita kunyumba kwa mayiyo ndikuyamba kumunena kuti akudwala matenda a AIDS ndipo wafalitsa matendawo kwa amuna ochuluka mderalo.

 

Related posts

Malawi ranks high in Esophageal Cancer

Romeo Umali

Questions over authenticity of Bushiri’s extradition request

Rabson Kondowe

Two win big in TNM’s Tikolore Promotion

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.