Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani

Thupi la Dr Chilima aliyika m’manda

Thupi la wachiwiri kwa mtsogoleri wadziko lino, malemu Dr Saulos Chilima, aliyika m’manda pamudzi wa Mbirimtengelenji pa Nsipe m’dera la Senior Chief Inkosi Champiti m’boma la Ntcheu.

Mtsogoleri wa dziko lino, Dr Lazarus Chakwera, ndi amene anatsogolera aMalawi pamwambo oyika malemu Dr. Chilima m’manda.

Asilikali a Malawi Defence Force anaomba mizinga khumi, isanu ndi inayi popereka ulemu wawo otsiliza kwa malemuwa.

Dr Chakwera ndi mayi Monica Chakwera anakayalanso nkhata pa mwambowu.

Wamkulu wa asilikali, a nkhondo General Paul Valentino Phiri pamodzi ndi wamkulu wa apolisi, a Merlyne Yolamu, onse anakapereka nawo ulemu otsiriza.

Atsogoleri akale a dziko lino, Dr Bakili Muluzi ndi Professor Peter Mutharika pamodzi ndi mayi Getrude Mutharika, anakapelekanso ulemu otsiriza.

Wachiwiri kwa mtsogoleri wopuma, a Khumbo Hastings Kachali, Chief Justice Rizine Mzikamanda, mlembi wamkulu mu ofesi ya Prezidenti ndi Kabineti komanso nduna za boma mwa ena ambiri, nawonso anachita motero.

Print Friendly, PDF & Email

Author

  • Mayeso Chikhadzula joined MBC in 2006, he's an Investigative Journalist and Principal Reporter. He's also a News Anchor, Presenter, and producer.

Related posts

Illovo ithandiza okhudzidwa ndi kusefukira kwa madzi ku Nkhotakota

MBC Online

Bushiri apereka chakudya kwa ovutika ku Mangochi

Rabson Kondowe

Apolisi amanga anthu 696

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.