Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Ntchito yopanga ziphaso ku Mangochi ikutheka

Anthu okhala m’boma la Mangochi ndi maboma ena ku chigawo cha kumvuma tsopano ali ndi kuthekera kopangitsa zitupa zoyendera nthambi ya Immigration italengeza kuti iyambiranso kugwira ntchito yopereka ziphaso ku ofesi zake m’boma la Mangochi kuyambira pa 20 August, chaka chino.

Ofalitsa nkhani ku nthambiyi, a Wellington Chiponde, anati kuyambiranso kwa ntchitoyi kuthandiza anthu okhala m’madera akumvuma kwa dziko lino kuti adzilembetsa komanso kulandira ziphasozi mosavuta.

Izi zikutanthauza kuti tsopano ofesi zonse za nthambiyi zayamba kugwira ntchito.

“Ife takhala tikunena kuti tikuchita chothekera kuti ntchito yopereka zitupa m’dziko muno izigwirika mwachangu ndipo momwe zateremu ndiye kuti zonse zili bwino,” a Chiponde anatero.

Mangochi ndi limodzi mwa ma boma omwe nzika zake zimakonda kupita maiko akunja monga ku South Africa kukachita malonda komanso kugwira ntchito.

Related posts

Aphungu awiri a DPP agwirana pakhosi

Romeo Umali

Tilimbikitse ufulu wa anthu omwe ali ndi ulumali— MACODA

Mayeso Chikhadzula

Chionetsero cha zaulimi chapindulira alimi — TRADE Programme

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.