Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Politics

Aphungu awiri a DPP agwirana pakhosi

Phungu wa Blantyre City South East, Sameer Suleman wapatsidwa chilango kuti asabwerenso ku Nyumba ya Malamulo kwa nthawi yonse yomwe aphungu adzakhale akukumana (Full sitting).

Pamene Phungu wa chipani cha DPP Zomba Chisi Mark Botomani wapatsidwa chilango cha masiku awiri kuti asalowe mnyumbayi kaamba koti amayankhulabe pamene wachiwiri kwa wachiwiri wa Spikala wa Nyumba ya Malamulo anawauza kuti akhale pansi.

Mpungwepungwewu unabwera pamene a Suleman anagwira pakhosi komanso kumenya khofi phungu mzawo a Mark Botomani mnyumbayi.

Ngakhale mkulu wa aphungu a chipani cha DPP, a Mary Thom Navicha, anayesela kuleletsa, a Suleman anapitilizabe kulalata mnyumbayi ndikuwakankhanso a Navicha.

Poyankhulapo, Spikalayu anati aka ndikachitatu kuti a Suleman achite chisokonezo mnyumbayi mchifukwa chake awapatsa chilango chokhwima.

Pakali pano Nyumbayi yayamba yaimitsa kaye zokambilana zake.

 

Related posts

‘Siyani kufalitsa nkhani zabodza pa imfa ya Dr Chilima’

Romeo Umali

CHAKWERA CALLS FOR PROTECTION OF MINERAL RESOURCES

MBC Online

Court grants bail to Bullets’ bus vandalisers 

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.