Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Mayi akagwira ukayidi kwa zaka ziwiri atavulaza mamuna wake

Bwalo la milandu m’boma la Mangochi lalamula a Alice Mailosi azaka 31 kuti akagwire ukayidi wakalavula gaga kwa zaka ziwiri chifukwa chovulaza mamuna wawo, yemwe sanatchulidwe dzina, pomuthira madzi owira atasemphana pankhani zachikondi.

Oweruza milandu, a Muhammad Chande, anapereka chilangochi kuti ena atengerepo phunziro.

Ofalitsa nkhani pa Polisi ya Mangochi, a Amina Tepani Daudi, ati mlanduwu unachitika pa 8 March chaka chino pamene a Mailosi amaganizira kuti mamuna wawo amakumanabe ndi bwenzi lawo lakale yemwe dzina lake ndi Alice Ida wa zaka 21.

Related posts

CHAKWERA ADDRESSES UN SDG SUMMIT

Blessings Kanache

Bambo amangidwa atagwilira, kupha mlamu wake

Romeo Umali

Parliament calls for transparency and accountability of govt resources

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.