Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Mayi akagwira ukayidi kwa zaka ziwiri atavulaza mamuna wake

Bwalo la milandu m’boma la Mangochi lalamula a Alice Mailosi azaka 31 kuti akagwire ukayidi wakalavula gaga kwa zaka ziwiri chifukwa chovulaza mamuna wawo, yemwe sanatchulidwe dzina, pomuthira madzi owira atasemphana pankhani zachikondi.

Oweruza milandu, a Muhammad Chande, anapereka chilangochi kuti ena atengerepo phunziro.

Ofalitsa nkhani pa Polisi ya Mangochi, a Amina Tepani Daudi, ati mlanduwu unachitika pa 8 March chaka chino pamene a Mailosi amaganizira kuti mamuna wawo amakumanabe ndi bwenzi lawo lakale yemwe dzina lake ndi Alice Ida wa zaka 21.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Real estate firm support surveyors’ indaba

MBC Online

CHAKWERA ASSENTS TO 4 BILLS

Blessings Kanache

First Couple joins Way of the Cross Procession

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.