Malawi Broadcasting Corporation
Development Health Local Local News Nkhani

Makina othandiza vuto la impso akonzedwa ku QECH

Chipatala cha Queen Elizabeth (QECH) munzinda wa Blantyre chati tsopano makina ake atatu mwa asanu othandiza anthu amene ali ndi vuto la impsyo ayamba kugwira ntchito.

Mmodzi mwa akuluakulu pa chipatalachi, Dr William Peno, anena izi pamene wachiwiri kwa nduna yoona za umoyo, a Noah Chimpeni, anakayendera zipinda zimene amasamalirako anthuwo.

Dr Peno ati kuoonongeka kwa makinawo kunachititsa kuti odwala ena adziwatumiza ku chipatala cha Kamuzu Central munzinda wa Lilongwe.

Iwo anati izi zimachititsa kuti adziwononga ndalama zochuluka zedi chifukwa chipatala cha QECH chimalandira anthu pafupifupi makumi awiri pa sabata omwe amakhala ndi vuto la impsyo.

Pakadali pano, a Dr Peno ati akuyembekezera kuti makina enawo ayambanso kugwira ntchito pamathero a sabata ino kaamba kakuti akuwakonza.

Masiku angapo apitawo, makinawa anasiya kugwira ntchito ndipo a Chimpeni atayendera zipindazo m’mbuyomu adalonjeza kuti boma lilowelerapo.

Related posts

Karonga climate smart participants for expansion of beneficiary coverage

Rabson Kondowe

Mzuzu Catholic Diocese urges Malawi to seek God’s intervention

MBC Online

Ntchito yomanga malo opereka madzi ku Mangochi yafika theka – SWRB

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.