Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani

Boma lakhudzika ndi ngozi ya ku Kasungu

Ofalitsa nkhani za boma, a Moses Kunkuyu, ati boma ndi lokhudzidwa kwambiri ndi imfa za anthu 26 omwe amwalira pangozi ya galimoto m’boma la Kasungu lero m’mawawu.

Ngoziyi yachitika pamene minibus yomwe imachokera kwa Jenda kupita ku Lilongwe inawombana ndi galimoto lalikulu lonyamula mafuta yomwe inagundanso munthu wina yemwe amapalasa njinga zomwe zinapangitsa kuti pabuke moto woopsa.

A Kunkuyu anati mtsogoleri wa dziko lino, Dr Lazarus Chakwera pamodzi ndi mayi wa pfuko lino, Madam Monica Chakwera, ali ndi chisoni chachikulu ndi imfa ya anthuwa.

Iwo ati Dr Chakwera alamula kuti achite chilichonse chothekera popereka thandizo lofunikira mabanja onse oferedwa pa ngoziyi ndipo anati boma liwonetsetsa kuti onse atisiyawa apatsidwe ulemu woyenera.

 

Related posts

Mangochi communities describe Social Cash Transfer Programme as life-changer

MBC Online

AEJ conference wraps up with new leadership

MBC Online

WESM calls for participation in the fight against climate change

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.