Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani

Dziko la Malawi latsegula ofesi ya ukazembe ku Israel

Dziko la Malawi latsegula ofesi ya ukazembe m’dziko la Israel kaamba kofuna kuti dziko lino lipindule ndi ntchito za ulimi ndi mtengatenga, mwa zina.
A Nancy Tembo omwe ndi nduna yoona za ubale wa dziko lino ndi maiko a kunja ati ofesiyi ndi yofunika chifukwa padakali pano achinyamata ambiri a m’dziko muno ali m’dziko la Israel ndipo ndikofunika kuti mdzikolo mukhale ofesiyi.
Malingana ndi a Tembo, ofesiyi ikhala mu mzinda wa Tel Aviv.
Nduna yoona za ntchito a Agness Nyalonje komanso nduna yofalitsa nkhani a Moses Kunkuyu komanso nthumwi zina za dziko la Malawi ku Israel ndi ena ambiri, anali limodzi pamene ofesiyi amayitsegula.

Related posts

Thyolo ramps up efforts to bolster Covid-19 Vaccine uptake

Romeo Umali

BANKING AMENDMENT BILL NEEDS FURTHER CONSULTATIONS

MBC Online

‘Masewero opalasa njinga ali ndi tsogolo’

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.