Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani

Dziko la Malawi latsegula ofesi ya ukazembe ku Israel

Dziko la Malawi latsegula ofesi ya ukazembe m’dziko la Israel kaamba kofuna kuti dziko lino lipindule ndi ntchito za ulimi ndi mtengatenga, mwa zina.
A Nancy Tembo omwe ndi nduna yoona za ubale wa dziko lino ndi maiko a kunja ati ofesiyi ndi yofunika chifukwa padakali pano achinyamata ambiri a m’dziko muno ali m’dziko la Israel ndipo ndikofunika kuti mdzikolo mukhale ofesiyi.
Malingana ndi a Tembo, ofesiyi ikhala mu mzinda wa Tel Aviv.
Nduna yoona za ntchito a Agness Nyalonje komanso nduna yofalitsa nkhani a Moses Kunkuyu komanso nthumwi zina za dziko la Malawi ku Israel ndi ena ambiri, anali limodzi pamene ofesiyi amayitsegula.

Related posts

2024/25 cotton marketing season opens

Romeo Umali

Former MP equips Kanjeza Community Day Secondary School with solar panels

MBC Online

Ndi mlandu kugulitsa, kuononga ndalama zachitsulo — Banki ya Reserve

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.