Malawi Broadcasting Corporation
Development Local News Nkhani Sports Sports

Dedza Dynamos yatola chikwama

Timu ya Dedza Dynamos tsopano izidziwika kuti Premeir Bet Dedza Dynamos kutsatira m’gwirizano umene yakhazikitsa ndi kampani ya Premier Bet wa ndalama zokwana K100 million wa chaka chimodzi.

Ngati mbali imodzi yowalimbikitsa osewera a timuyi, Premier Bet idzipereka ndalama zokwana K100,000 kwa osewera bwino pa mwezi ndipo K500,000 idzipita kwa osewera bwino pa chaka.

Otsatira komanso kuchemelera timuyi ndi amene adzisankha osewerawa ndipo ndalama yokwana K200,000 idzipita kwa ochemelera amene waonetsa chikondi ku timuyi.

Olemba : Amin Mussa

Related posts

RCRP-2 to bolster Malawi’s infrastructure against climate shocks

McDonald Chiwayula

‘Osagulitsa fodya kwa mavenda’

MBC Online

Depositors’ protection agency to launch next week

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.