Malawi Broadcasting Corporation
Development Local News Nkhani Sports Sports

Dedza Dynamos yatola chikwama

Timu ya Dedza Dynamos tsopano izidziwika kuti Premeir Bet Dedza Dynamos kutsatira m’gwirizano umene yakhazikitsa ndi kampani ya Premier Bet wa ndalama zokwana K100 million wa chaka chimodzi.

Ngati mbali imodzi yowalimbikitsa osewera a timuyi, Premier Bet idzipereka ndalama zokwana K100,000 kwa osewera bwino pa mwezi ndipo K500,000 idzipita kwa osewera bwino pa chaka.

Otsatira komanso kuchemelera timuyi ndi amene adzisankha osewerawa ndipo ndalama yokwana K200,000 idzipita kwa ochemelera amene waonetsa chikondi ku timuyi.

Olemba : Amin Mussa

Related posts

University students back Ministry of Higher Education formation

Rabson Kondowe

CENTRE FOR AGRICULTURAL TRANSFORMATION BAGS INTERNATIONAL AWARD

MBC Online

Chakwera to open trade fair

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.