Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Politics

Musamvere andale abodza, ogawa mitundu — Chimwendo Banda

Mlembi wa mkulu wa chipani cha Malawi Congress (MCP), a Richard Chimwendo Banda, wachenjeza aMalawi kuti asamvere atsogoleri andale amene adayeserapo koma adakanika kutukula dziko lino.

A Chimwendo Banda amayankhula izi pa msonkano wa ndale kwa Mgona munzinda wa Lilongwe, kumene anati ntchito za boma lapano ndi zowonekeratu.

Iwo anati m’mbuyomu, aMalawi monga achigawo chakumpoto adanamizidwapo ndi boma la nthawiyo kuti liwamangira bwalo la ndege ku Mzuzu komanso sukulu ya ukachenjede ya Mombera.

A Chimwendo Banda anatinso mtsogoleri wa dziko lino, Dr Lazarus Chakwera, waonetsa kuti akuyika mtima pa zinthu zofunika m’dziko muno ndipo n’kofunika kuti aMalawi akhale pambuyo pake.

Olemba: Isaac Jali

Related posts

Increased digital banking uptake key to paperless transactions

Rabson Kondowe

Tililire Mulungu — Bishop Nyirenda

Romeo Umali

Petroleum importers provides safe water to Linyangwa Health Centre

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.