Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Anthu ayamikira ntchito zabwino za Kapusa

Malemu Geoffrey Kapusa waikidwa mmanda lero kumudzi kwawo.

Anthu osiyanasiyana anali nawo pa mwambowu, ndipo onse anati Geoffrey wasiya mbiri yotamandika pankhani zoulutsa mawu pakanema m’dziko muno.

Geofrey “Mr Splash” Kapusa anamwalira dzana pachipatala cha Queen Elizabeth Central mu mzinda wa Blantyre.

Iye anadziwika kwambiri ndikuthandiza oyimba kuti adziwike kudzera mu programme yake ya Music Splash pa kanema ya MBC, kuyambira pomwe inkayamba kumene ngati TVM.

Geoffrey, yemwe anabadwa m’chaka cha 1971, wasiya ana atatu.

Related posts

COMESA Competition Commission reaches out to Zoe Foundation

Mayeso Chikhadzula

CHIWEMBE FOR BLANTYRE CENTENARY CRUSADE COMMENCES SUNDAY

MBC Online

Small-scale irrigation boosts food security for Dedza farmers

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.