Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Anthu ayamikira ntchito zabwino za Kapusa

Malemu Geoffrey Kapusa waikidwa mmanda lero kumudzi kwawo.

Anthu osiyanasiyana anali nawo pa mwambowu, ndipo onse anati Geoffrey wasiya mbiri yotamandika pankhani zoulutsa mawu pakanema m’dziko muno.

Geofrey “Mr Splash” Kapusa anamwalira dzana pachipatala cha Queen Elizabeth Central mu mzinda wa Blantyre.

Iye anadziwika kwambiri ndikuthandiza oyimba kuti adziwike kudzera mu programme yake ya Music Splash pa kanema ya MBC, kuyambira pomwe inkayamba kumene ngati TVM.

Geoffrey, yemwe anabadwa m’chaka cha 1971, wasiya ana atatu.

Related posts

MCP gears for 2025 Elections

Mayeso Chikhadzula

NICE sensitises traders on engagement with council officials

Rabson Kondowe

Chakwera hails global efforts to boost electricity access in Africa

Mayeso Chikhadzula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.