Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

A Chakwera asankha a Mazalale ngati mlembi wa mapulani achitukuko

Mtsogoleri wa dziko lino Dr. Lazarus Chakwera wasankha a Jacob Mazalale ngati mlembi mu unduna wa zachuma oona za mapulani achitukuko.

A Mazalale, amene ndi mphunzitsi wazachuma pa sukulu yaukachenjede ya Unima ku Zomba, adzikayang’ana nkhani zokhudza mapulani achitukuko ndi chuma ku undunawu.

Mneneri ku ofesi ya mlembi wa mtsogoleri wa dziko lino ndi nduna zake, a Robert Kalindiza, atsimikiza za nkhaniyi.

A Kalindiza ati Dr Chakwera asankha a Mazalale ndicholinga chofuna kuwonetsetsa kuti chuma cha dziko lino chipitilire kubwelera mchimake.

 

Related posts

Nduna yazofalitsa nkhani ipereka lipoti la ngozi ya ndege ya Chichewa

Romeo Umali

DoDMA ilimbikitsa chitukuko cha madzi aukhondo

Romeo Umali

Ntchito za manja zikuthandiza kusintha miyoyo ya achinyamata

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.