Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani

President Chakwera awonekera m’nyumba ya malamulo

Mtsogoleri wa dziko lino, Dr Lazarus Chakwera, lero akawonekera ku nyumba ya malamulo ndikukayankha mafunso kuchokera kwa aphungu anyumbayi.

Potsimikiza izi, mneneri wa Boma, a Moses Kunkuyu, wati President Chakwera akawonekera ku nyumbayi pokwaniritsa malonjezo ake woti adzakhala wotumikira anthu a m’dziko muno poyankha mafunso kudzera kwa aphungu awo.

Mtsogoleri wadziko linoyu akakhala ali ku nyumba ya malamulo masana ano kuyambira nthawi ya 2 koloko.

Wolemba: Timothy Kateta

#MBCOnlineServices

Related posts

Malawi International Arbitration Centre gets financial boost

Rabson Kondowe

JSC launches corruption investigation

MBC Online

Nkhoma helps KB move third

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.