Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

‘Sankhani moyenera zokaphunzira ku university’

Phungu wadera la Kumachenga m’boma la Lilongwe a Ezra Ching’onga adandaula kuti ophunzira ambiri omwe amalemba mayeso a MSCE mdera lake sasankhidwa kupita ku university chifukwa amalephera kusankha moyenera ma programme aku university mogwirizana ndi momwe akhonzera mayeso a MSCE.

“Ophunzira mdera lathu amakhonza mayeso a MSCE koma sapita ku sukulu zaukachenjede. Chitsanzo ena amakhoza  ndi ma points oposa makumi awiri, koma akufuna maphunziro azasayansi  monga engineering, a NCHE angamutenge ?” anadandaula choncho a Ching’onga.

Iwo anati kusankha moyenera kungatheke ndi thandizo la aphunzitsi komanso makolo amene ali ndikuthekera.

Iwo ayankhula izi pamwambo otsanzikana ndi ophunzira a Form 4 apa sukulu ya Njewa Community Day.

Mphunzitsi wamkulu pa sukulupo a Emmanuel Mponda ati ayesetsa kuwunikila achinyamatawo pa zisankho zoyenera.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

NCHE revokes accreditation for Skyway, Millennium Universities

MBC Online

VIHEMA calls for collective effort in making deaf-blindness visible

Charles Pensulo

STREAMS Programme transforms WASH in Rumphi health facilities

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.