Mtsogoleri wa dziko lino, Dr Lazarus Chakwera, lero apita m’boma la Mzimba kumene ayendere ntchito yomanga bwalo lazamasewero la M’mbelwa kudzanso ofesi za khonsolo ya M’mbelwa m’bomalo.
Dr Chakwera akafikanso kulikulu la Inkosi yamakhosi M’mbelwa.
Mtsogoleri wa dziko linoyu akucheza m’chigawo chakumpoto ndikuyendera ntchito za chitukuko zosiyanasiyana.

