Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Kamlepo wayamikira Chakwera pa chitukuko

Phungu wa dera lakummawa kwa boma la Rumphi, a Kamlepo Kalua, ayamikira mtsogoleri wa dziko lino, Dr Lazarus Chakwera, chifukwa cholora bungwe la MACRA kuti limange chipinda chatsopano chophunzitsira luso la computer pa Sukulu ya Jalawe CDSS.

Kalua wayankhula izi pamene bungweli limakhazikitsa ntchitoyi ku Rumphi.

Iye anati chitukukocho chibwera limodzi ndimagetsi pasukulupo ponena kuti makina a computer amafuna magetsi ndiye sizingatheke kuti ayike makinawa pamalo pamene palibe magetsi.

Ena mwa ana ophunzira ku Jalawe CDSS

Bungwe la MACRA likumanga zipinda zophunzitsira makina a computer musukulu 75 za m’dziko muno,  ntchito imene ikuyembekezeka kutha m’miyezi itatu ikubwerayi ndipo igwilitsa ntchito ndalama zokwana K6 billion.

 

Olemba: Hassan Phiri

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

MARANATHA ACADEMY DECORATES OUTSTANDING FORM 4 STUDENTS, TEACHERS

MBC Online

Aphungu awiri a DPP agwirana pakhosi

MBC Online

MATINDI FAULTED

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.