Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Kamlepo wayamikira Chakwera pa chitukuko

Phungu wa dera lakummawa kwa boma la Rumphi, a Kamlepo Kalua, ayamikira mtsogoleri wa dziko lino, Dr Lazarus Chakwera, chifukwa cholora bungwe la MACRA kuti limange chipinda chatsopano chophunzitsira luso la computer pa Sukulu ya Jalawe CDSS.

Kalua wayankhula izi pamene bungweli limakhazikitsa ntchitoyi ku Rumphi.

Iye anati chitukukocho chibwera limodzi ndimagetsi pasukulupo ponena kuti makina a computer amafuna magetsi ndiye sizingatheke kuti ayike makinawa pamalo pamene palibe magetsi.

Ena mwa ana ophunzira ku Jalawe CDSS

Bungwe la MACRA likumanga zipinda zophunzitsira makina a computer musukulu 75 za m’dziko muno,  ntchito imene ikuyembekezeka kutha m’miyezi itatu ikubwerayi ndipo igwilitsa ntchito ndalama zokwana K6 billion.

 

Olemba: Hassan Phiri

Related posts

Chakwera condemns corruption in developmental initiatives

Rabson Kondowe

Peter Falvey Foundation pledges more water projects

Rabson Kondowe

PSPTF launches strategic plan

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.