Malawi Broadcasting Corporation
Development Local News Nkhani

Ndine otetezedwa tsopano, watero mnyamata waku Salima

Mnyamata wochokera dera lamfumu yaikulu Mwanza m’boma la Salima, Chinsinsi Luka, yemwe ndi alubino, tsopano wati ndiwosangalala kamba kanyumba yomwe boma lamumangira.

Nyumbayi ndimbali imodzi ya ntchito yomanga nyumba kwa anthu achi alubino yomwe mtsogoleri wadziko lino anaikhazikitsa.

Unduna wa zamalo komanso unduna owona kuti pasamakhale kusiyana pakati pamayi ndi abambo apereka nyumbayi kwanyamatayu ndi banja lake lero.

Nduna yoona kuti pasamakhale kusiyana pakati pa amayi ndi abambo, a Jean Sendeza, alimbikitsa anthu m’dziko muno kuteteza anthu achi alubino.

Ndipo nduna ya zamalo, a Deus Gumba, ayamikira ntchito yamtunduwu, kunena kuti ndichitsimikizo kuti boma limaganizira umoyo wa aliyense m’dziko muno.

Pakali pano, boma lamanga nyumba za anthu achi alubino m’dziko muno zokwana 65.

 

Related posts

Airtel Malawi enhances security to combat mobile money fraud

Rabson Kondowe

Malawi Red Cross calls for responsible reporting during disasters

Rabson Kondowe

Social Media misinformation worries government

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.