Malawi Broadcasting Corporation
Development Local News Nkhani

Ndine otetezedwa tsopano, watero mnyamata waku Salima

Mnyamata wochokera dera lamfumu yaikulu Mwanza m’boma la Salima, Chinsinsi Luka, yemwe ndi alubino, tsopano wati ndiwosangalala kamba kanyumba yomwe boma lamumangira.

Nyumbayi ndimbali imodzi ya ntchito yomanga nyumba kwa anthu achi alubino yomwe mtsogoleri wadziko lino anaikhazikitsa.

Unduna wa zamalo komanso unduna owona kuti pasamakhale kusiyana pakati pamayi ndi abambo apereka nyumbayi kwanyamatayu ndi banja lake lero.

Nduna yoona kuti pasamakhale kusiyana pakati pa amayi ndi abambo, a Jean Sendeza, alimbikitsa anthu m’dziko muno kuteteza anthu achi alubino.

Ndipo nduna ya zamalo, a Deus Gumba, ayamikira ntchito yamtunduwu, kunena kuti ndichitsimikizo kuti boma limaganizira umoyo wa aliyense m’dziko muno.

Pakali pano, boma lamanga nyumba za anthu achi alubino m’dziko muno zokwana 65.

 

Related posts

CROSS-BORDER TRADERS HAIL ONE-STOP BORDER POST

McDonald Chiwayula

MW, OPEC FUND SIGN FINANCIAL AGREEMENTS

McDonald Chiwayula

CSO to lobby for funding for Salima Sugar Company’s expansion

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.