Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani

Prezidenti Chakwera akhala nawo pa mwambo operekeza maliro

Anthu ochuluka asonkhana ku nyumba ya chisoni ya Sunset Funeral Services ku Kanengo munzinda wa Lilongwe komwe pali chikonzero chonyamula ena mwa matupi a anthu omwe adafa pangozi ya ndege limodzi ndi wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino, malemu Dr Saulos Chilima.

Pali chiyembekezo choti pa mwambowu pakhalanso mwambo wa Misa poremekeza mzimu wa mayi Patricia Shanil Dzimbiri, omwe anaakhalapo mayi wa dziko lino zaka za mmbuyomu.

Prezidenti wa dziko lino, Dr Lazarus Chakwera, komanso mayi wa dziko lino, Madam Monica Chakwera, akuyembekezeka kukhala nawo pamwambowu.

 

Related posts

NATIONAL PRODUCT MAGAZINE GETS REGIONAL RECOGNITION

Mayeso Chikhadzula

NLGFC Board impressed by quality of projects in Rumphi

Alinafe Mlamba

‘Boma likukumana ndi zovuta polimbana ndi mchitidwe wa nkhanza kwa anthu achikulire’

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.