Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Amagulitsa mwana wake wazaka zitatu

Apolisi ku Nkhunga m’boma la Nkhotakota amanga amuna awiri powaganizira kuti amatsatsa malonda a mwana wazaka zitatu.

Mneneri wapolisi ya Nkhunga, Andrew Kamanga, wati amunawo ndi Pilirani Thumba wazaka  38 yemwe ndi bambo wamwanayo komanso Yohane Watch wazaka 48.

A Kamanga ati apolisiwo anatsinidwa khutu ndi anthu ena kuti pali abambo ena omwe akugona pamalo ogona alendo pasitolo za pa Dwangwa ndipo akugulitsa mwana.

Apolisiwo atafika pamalopo, anapeza amunawo ndipo atawafunsa anavomera kuti akugulitsa mwanayo.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Sign language can develop Malawi — SLID

Juliana Mlungama

Awanjata pogulitsa mankhwala owopsa

Blessings Kanache

NGO-GCN denounce political violence

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.