Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Amagulitsa mwana wake wazaka zitatu

Apolisi ku Nkhunga m’boma la Nkhotakota amanga amuna awiri powaganizira kuti amatsatsa malonda a mwana wazaka zitatu.

Mneneri wapolisi ya Nkhunga, Andrew Kamanga, wati amunawo ndi Pilirani Thumba wazaka  38 yemwe ndi bambo wamwanayo komanso Yohane Watch wazaka 48.

A Kamanga ati apolisiwo anatsinidwa khutu ndi anthu ena kuti pali abambo ena omwe akugona pamalo ogona alendo pasitolo za pa Dwangwa ndipo akugulitsa mwana.

Apolisiwo atafika pamalopo, anapeza amunawo ndipo atawafunsa anavomera kuti akugulitsa mwanayo.

Related posts

Israel donates desks to LCC

Romeo Umali

FAM ikufuna abale ambiri kumpira wa miyendo

Alinafe Mlamba

2,500 Green Innovators equipped with skills, tools

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.