Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Sports Sports

Osewera watsopano wa Wanderers Tanjong apezeka kumathero asabatayi

Timu ya Mighty Mukuru Wanderers yati yapereka kalata ku nthambi yoona zolowa komanso kutuluka m’dziko muno, zofuna kupeza chilolezo kuti katswiri wawo wakutsogolo ochokera ku Cameroon, Sama Tanjong, ayambe kusewera m’dziko muno.

Tanjong, yemwe posachedwapa wasayina contract yazaka ziwiri ndi Wanderers, analephera kupezeka pamasewero atimuyi ndi FCB Nyasa Big Bullets kaamba kakuti alibe chilolezo chogwira ntchito mdziko muno.

Mkulu wa Wanderers, Panganeni Ndovi, watsimikiza kuti pali kuthekera kuti osewerayu apezeka pamasewero atimuyi kumathero asabatayi

Tanjong, yemwe anayambila mpira wake ku timu yachisodzera ya First Sport ku Cameroon, wasewerako matimu amayiko a Democratic Republic of Congo ndi South Africa, ndipo wagoletsa zigoli 112.

Wolemba: Praise Majawa

Related posts

Chinese EV manufacturer targets Zimbabwe, Malawi in Africa expansion drive

MBC Online

Chakwera ndi chiyembekezo cha dziko lino – Chimwendo Banda

Rabson Kondowe

Chitipa Council to mainstream disability issues in development plans

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.