Malawi Broadcasting Corporation
Entertainment Local Local Music News Nkhani

Muzilimbikira ngakhale mutakumana ndi mavuto — Sife

Oyimba Silvia ‘Sife’ Sande, amene amadziwika bwino ndi nyimbo yake yotchedwa Kumaloto, walimbikitsa anthu m’dziko muno kuti ngakhale atakumana ndi mavuto adzingolimbikira ndipo asamadziyerekeze ndi ena.

Iye wati anthu ambiri amene amaoneka ngati opanda mavuto nawonso amakhala akukumana ndi mikwingwirima yosiyanasiyana.

Chifukwa cha ichi, Sife wayimba nyimbo yatsopano yotchedwa ‘Amafukeni’ pamodzi ndi K Banton komanso Jolasto ndipo ndi yolimbikitsa anthu.

Katswiri oyimbayu anapemphanso anthu kuti asamaganize zochotsa moyo wawo chifukwa nyengo iliyonse imakhala ndi pothera pake.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

KIA Police celebrates Christmas with children

MBC Online

School Feeding Programme retains girls in school

McDonald Chiwayula

Central Region Prison Headquarters awards outstanding formations

Yamikani Simutowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.