Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani

Nduna yazofalitsa nkhani ipereka lipoti la ngozi ya ndege ya Chichewa

Nduna ya zofalitsa nkhani yomwenso ndi mneneri wa boma, a Moses Kunkuyu akuchititsa msonkhano wa atolankhani ku Lilongwe pa lipoti la ngozi ya ndege yomwe inapha yemwe anali wachiwiri kwa mtsogoleri wadziko lino Dr. Saulos Chilima ndi anthu ena asanu ndi atatu.

A Kunkuyu ati achititsa msonkhanowu pofuna kupereka uthenga omwe uli mu lipotili muchiyankhulo chomwe anthu onse mdziko muno angamvetse chomwe ndi Chichewa.

Kampani yomwe inachita kafukufuku wa chomwe chinachititsa ngoziyi ya German Federal Bureau of Aircraft Accident Investigation (BFU) inatulutsa lipoti loyambilira la ngoziyi lachisanu pa 31 August.

Pakadali pano ndunayi ikuwerenga lipotili lomwe alitanthauzira mchichewa.

 

Related posts

Magetsi ndi awa koma asamaleni- Matola

Rabson Kondowe

TUMBUKA HERITAGE ASSOCIATION EMBARKS ON DOCUMENTATION PROJECT

MBC Online

‘Anthu achikulire akhale ndi mwayi ovota’

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.