Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani

MRCS yapereka madzi a m’mipopi ku Karonga

Bungwe la Malawi Red Cross Society (MRCS) lapereka madzi a m’mipopi kwa anthu a m’dera la mfumu yayikulu Mwirang’ombe m’boma la Karonga pofuna kulimbikitsa ukhondo.

Madziwa ndi odalira mphamvu ya dzuwa ndipo pali mipopi 16 yomwe yayikidwa m’malo osiyanasiyana.

M’modzi mwa akuluakulu abungweli, a Dan Nyirenda, ati madziwa afikira mabanja 480 kuphatikizapo sukulu ya pulayimale ya Ngara, chipatala cha ching’ono cha m’deralo komanso malo ochitira malonda.

Yemwe anayimira Bwanamkubwa wa bomali, a Yaz Nyirenda, anati anthu m’derali amavutika kaamba kosowa madzi abwino ndipo thandizoli lithetsa vutoli.

M’modzi mwa amayi okhala m’mudzi mwa agulupu a Muyeleka, a Watipaso Simeza, anathokoza chitukukochi.

“Poyamba timatenga madzi kunyanja komwe ndi kutali komanso madziwo sanali awukhondo,” a Simeza anatero.

Chifukwa chosowa madzi awukhondo, chaka chatha chokha anthu 63 akhala akugwidwa ndi nthenda ya Cholera ndipo asanu ndi awiri anafa ndi nthendayi.

Olemba: George Mkandawire

Related posts

Commentators agitate for bank notes replacement to punish looters

Romeo Umali

STAKEHOLDERS CALL FOR ADDED INVESTMENT TO EXPAND PALLIATIVE CARE INTERVENTIONS

Secret Segula

TNM records 15 percent revenue growth in 2023

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.