Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Mankhwala ophera tizilombo a chlorine samalepheretsa kubereka

Boma lati mankhwala ophera tizilombo a chroline alibe vuto lirilonse pa umoyo ngakhalenso nkhani zokhudza ubereki.

Wachiwiri kwanduna yoona za madzi ndi ukhondo a Liana Kakhobwe Chapota anena izi pamwambo opereka mankhwala a chroline ku khonsolo ya boma la Balaka.

Ndunayi yati sizoona zomwe anthu ena akhala akunena kuti madzi omwe ayikamo mankhwala opha tizilombo monga chlorine amalepheretsa kubereka.

Mmau ake wapampando wabungwe la Evidence Action lomwe lapereka thandizoli Dr Annie Phoya ati ndicholinga cha bungweli kuthandiza Boma pa ntchito yake yopereka madzi abwino ndi aukhondo kwa a Malawi ambiri makamaka am’madera akumidzi.

Thandizoli ndila ndalama zokwana K26 million.

Related posts

NEEF yati ipitilira kuthandiza anthu

Romeo Umali

Ochita bizinesi zing’onozing’ono apindula mu mgwirizano wa NBM ndi kampani zina

Rabson Kondowe

Khosolo ya Lilongwe yakhazikitsa komiti yoona za bata ndi mtendere

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.