Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Kamtukule alowa chipani cha MCP

Nduna ya zokopa alendo a Vera Kamtukule omwe anali achipani cha UTM alowa chipani cha Malawi Congress.

Powalandira mchipanichi Mlembi Wamkulu mchipani cha MCP a Eisenhower Mkaka ati a Kamtukule sanasochere kaamba koti alowa chipani chomwe chilibe mwini koma mchipani cha m’Malawi aliyense.

A Mkaka ati chipani cha MCP chili chokonzeka kulandira aliyense yemwe watsimikiza mtima kulowa chipanichi.

Poyankhulapo a Kamtukule ati alowa chipanichi kaamba koti akufuna kuthandiza mtsogoleri wadziko lino  Dr Lazarus Chakwera pogwira ntchito yotukula dziko la Malawi.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Mtukula Pakhomo wam’mizinda ufika ku Lilongwe lachinayi

MBC Online

Lands Ministry asked to fast track construction of houses for people with albinism

MBC Online

Malawi calls for unified voice at LDCs Ministerial Meeting

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.