Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Kamtukule alowa chipani cha MCP

Nduna ya zokopa alendo a Vera Kamtukule omwe anali achipani cha UTM alowa chipani cha Malawi Congress.

Powalandira mchipanichi Mlembi Wamkulu mchipani cha MCP a Eisenhower Mkaka ati a Kamtukule sanasochere kaamba koti alowa chipani chomwe chilibe mwini koma mchipani cha m’Malawi aliyense.

A Mkaka ati chipani cha MCP chili chokonzeka kulandira aliyense yemwe watsimikiza mtima kulowa chipanichi.

Poyankhulapo a Kamtukule ati alowa chipanichi kaamba koti akufuna kuthandiza mtsogoleri wadziko lino  Dr Lazarus Chakwera pogwira ntchito yotukula dziko la Malawi.

 

Related posts

Chakwera wanyamuka kubwelera ku Lilongwe

Alinafe Mlamba

Printing of passports halted by cyber attacks

McDonald Chiwayula

Livingstonia Synod to plant more than 5 million trees

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.