Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Ifenso tikuthandiza pa ntchito zokopa alendo —Daza

Mmodzi wa anthu  ochita malonda ogulitsa zakudya zophika zachi Malawi a Aubrey Daza, amene ndi mwini wa malo odyera a Chanza Take Away m’boma la Ntcheu, wati nawo amalonda ang’ono ang’ono mgawo  lawoli akuthandiza pantchito  zokopa  alendo.

Iwo anena izi pomwe mwezi uno, dziko lino likukumbukira ntchito zokopa alendo.

A Daza ati pakadali  pano, a Malawi ambiri anamvetsesa ubwino wa kudya  zakudya zachikhalidwe, zimenenso zikuchititsa kuti ntchito zawo ngati amalonda zidziyenda bwino.

Mmodzi mwa anthu amene tinakumana nawo pa malowa, a Julius Phiri, amene anali pa ulendo ochokera mu mzinda wa Mzuzu, anati ndiokhutira ndi momwe malo ang’ono ang’ono ngati otere akulimbikitsira ntchito zokopa alendo pogulitsa zakudya zachiMalawi.

 

Wolemba: Geoffrey Chinawa ndi Chisomo Break

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Misuku Motorhino Eco Rally 2024 racing on Saturday

MBC Online

CHAKWERA TO UNVEIL DEVELOPMENT VISION FOR MWANZA

MBC Online

Budget presentation coming soon

Arthur Chokhotho
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.