Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Madam Chakwera afika ku mwambo okumbukira tsiku la anthu achialubino

Mayi wa pfuko lino Madam Monica Chakwera afika pa bwalo la masewero la m’boma la Rumphi komwe ali nawo pa mwambo okumbukira tsiku la anthu achialubino.

Mwazina, atafika pabwalopa, Madam Chakwera anayendera zionetsero zomwe akonza a mabungwe omwe akugwira ntchito zosiyanasiyana zothandiza anthuwa.

Nduna yoona za chisamaliro cha anthu a Jean Sendeza komanso nkulu wabungwe la United Nations m’dziko muno a Rabbacca Addah Donto  komanso anthu osiyanasiyana ndi akuluakulu aboma ali nawo pamwambowu.

Patha zaka khumi tsopano kuyambira pomwe dziko la Malawi linayamba kuchita nawo chikondwererochi.

 

Related posts

Chief, 12 others nabbed for assault

Rabson Kondowe

Philanthropist changes winner unveiling approach for her youth entrepreneurship booster initiative

Romeo Umali

COP 28 FOR CLEAN ENERGY

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.