Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

‘Lolemba ndi tchuthi’

Nduna yazofalitsa nkhani , a Moses Kunkuyu, ati  mtsogoleri wa dziko lino, Dr. Lazarus Chakwera, alamula kuti lolemba likudzali, limene lili tsiku loyika mmanda ku Ntcheu yemwe anali wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko, malemu Dr Saulos Chilima, likhale tsiku la tchuthi.

Iwo ati cholinga chake ndikufuna kuti aMalawi athe kulira maliro a Dr. Chilima.

A Kunkuyu alongosola izi kumsonkhano wa olembankhani kunyumba yamalamulo.

Mmau awo, iwo ati ku mwambowu kukapezekanso akuluakulu osiyanasiyana ochokera kunja kwa dziko lino monga ku Tanzania, Botswana ndi Mozambique.

 

Olemba Mirriam Kaliza

Related posts

VP to attend Human Resource Society of Malawi AGM

Romeo Umali

CDH Bank donates K5 million to two orphanages

Romeo Umali

Chakwera launches dry spell, floods response appeal

Mayeso Chikhadzula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.