Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

‘Lolemba ndi tchuthi’

Nduna yazofalitsa nkhani , a Moses Kunkuyu, ati  mtsogoleri wa dziko lino, Dr. Lazarus Chakwera, alamula kuti lolemba likudzali, limene lili tsiku loyika mmanda ku Ntcheu yemwe anali wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko, malemu Dr Saulos Chilima, likhale tsiku la tchuthi.

Iwo ati cholinga chake ndikufuna kuti aMalawi athe kulira maliro a Dr. Chilima.

A Kunkuyu alongosola izi kumsonkhano wa olembankhani kunyumba yamalamulo.

Mmau awo, iwo ati ku mwambowu kukapezekanso akuluakulu osiyanasiyana ochokera kunja kwa dziko lino monga ku Tanzania, Botswana ndi Mozambique.

 

Olemba Mirriam Kaliza

Related posts

RA, Stakeholders to relocate Muloza One Stop Border Post

Rabson Kondowe

Forest officer warns against deforestation in Likoma

Romeo Umali

Malawi among top ten governed countries in Africa

Blessings Kanache
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.