Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Politics

Khamu lakonzeka kumva mfundo za chitukuko ku Lilongwe

Anthu ochuluka akhamukira ku bwalo lamasewero la pa msika wa Area 24 ku Lilongwe komwe kukhale msonkhano wa chipani cha Malawi Congress (MCP).

Pakadali pano, zokonzekera zonse zatha pamene anthu akudikira mtsogoleri wadziko lino Dr Lazarus Chakwera kuti adzakhale nawo pa msonkhanowu.

Magule osiyanasiyana akuvinidwaa ndipo oyimba monga Skeffa Chimoto komanso Mlaka Maliro akusangalatsa anthu.

Akuluakulu achipani, aphungu anyumba yamalamulo, mafumu a m’boma la Lilongwe, anyamata, asungwana komanso amayi ndi abambo adzadza pa bwalo la Maseweroli.

Related posts

Mediation efforts to end truck drivers’ strike underway

MBC Online

12-year-old girl in urgent need of wheelchair

Romeo Umali

Trade Ministry to review cooperative development policy

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.