Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Mtukula Pakhomo wam’mizinda ufika ku Lilongwe lachinayi

Anthu okhala mu nzinda wa Lilongwe omwe analembetsa mu ndondomeko ya Mtukula Pakhomo wam’mizinda akuyembekezeka kulandira ndalamazi lachinayi, zomwe ndi K150,000 aliyense.

Anthu 22 339 alandira mu gawo loyamba pamene gawo lachiwiri, anthu 16 329 ndiwo adzalandire ndipo gawo lachitatu adzalandira ndi anthu amene atatsale omwe salandira mmagawo awiri oyambilira.

Malinga ndi unduna wa zachuma ndi mapulani, ndalamazi cholinga chake ndikuthandizira anthu osowa amene akukumana ndi mavuto a zachuma.

Ku Zomba, Blantyre komanso Mzuzu, anthu analandira kale ndalamazi.

Related posts

PROPHET SHEPHERD BUSHIRI AGAWA CHIMANGA M’MABOMA AKUM’MWERA KUMAPETO ASABATAYI

McDonald Chiwayula

Mabedi wavomereza kuti Flames ili mu gulu lovuta mu AFCON 2025

MBC Online

Ogwira mkayidi othawa adzilandira thumba lachimanga

Yamikani Simtowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.