Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani Technology

Kaneneni ku Polisi anthu akakulakwirani pa Intaneti — MACRA

Bungwe la MACRA la limbikitsa a Malawi kuti adzikamang’ala ku Polisi ngati anthu ena awalakwira kapena kuwachitira upandu pa masamba a mchezo komanso malo ena pa makina a intaneti, mkulu wa bungweli a Daudi Suleiman anatsimikiza.

Mkulu wa Nthambi ya Computer Emergency Response Team (CERT) ku MACRA, a Christopher Banda, ati izi zikudza pamene madando akuchuluka okhudza anthu amene amachita malonda komanso kuwonetsa luso lawo pa makinawa kuti a Polisi sakumathandiza mokwanira powateteza, zomwe zikuchititsa kuti ntchito yawo isapite patsogolo.

Mwa maupandu ena, ndi monga kutsegula ma accaount abodza pa masamba a mchezo ndi cholinga chofuna kuna,iza, kunyoza komanso kubera ndalama anthu osadziwa.

Olemba : Yamikani Makanga

Related posts

UNIMA, Huawei sign MoU on human development

Romeo Umali

Norwegian govt committed to ensuring Malawians register for votes

Rabson Kondowe

‘Her Power Net initiative key to transforming the youth’

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.