Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani Technology

Kaneneni ku Polisi anthu akakulakwirani pa Intaneti — MACRA

Bungwe la MACRA la limbikitsa a Malawi kuti adzikamang’ala ku Polisi ngati anthu ena awalakwira kapena kuwachitira upandu pa masamba a mchezo komanso malo ena pa makina a intaneti, mkulu wa bungweli a Daudi Suleiman anatsimikiza.

Mkulu wa Nthambi ya Computer Emergency Response Team (CERT) ku MACRA, a Christopher Banda, ati izi zikudza pamene madando akuchuluka okhudza anthu amene amachita malonda komanso kuwonetsa luso lawo pa makinawa kuti a Polisi sakumathandiza mokwanira powateteza, zomwe zikuchititsa kuti ntchito yawo isapite patsogolo.

Mwa maupandu ena, ndi monga kutsegula ma accaount abodza pa masamba a mchezo ndi cholinga chofuna kuna,iza, kunyoza komanso kubera ndalama anthu osadziwa.

Olemba : Yamikani Makanga

Related posts

MACRA donates 15 computers to Blantyre Teachers’ College

Romeo Umali

Increase safety net allocations – World Bank

Rabson Kondowe

Minister urges companies to invest in tourism sector

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.