Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News

Immigration iyamba kusindikiza ma Passport mawa

Ntchito yosindikiza ma Passport tsopano iyambanso mawa lachitatu ku Blantyre, Nthambi yoona zolowa ndikutuluka m’dziko muno, ya Immigration, yatsimikiza zimenezi.

Mneneri wa nthambiyi, a Wellington Chiponde, ati anthu onse ofuna ziphaso zoyendera, tsopano atha kuyamba kupita ku likulu la nthambiyi ku Blantyre kukapeza ziphasozi kuyambira tsikuli.

A Chiponde athokoza anthu m’dziko muno kamba kopilira pa nthawi imene nthambiyi imakonza zinthu kuti ziyambenso kuyenda bwino.

Anthu ofuna ziphaso akhala akumakatenga ziphasozi ku Lilongwe a Immigration atasiya kusindikiza ku Blantyre atathetsa mgwirizano ndi kampani yomwe inkapanga ziphasozi mmbuyomu.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

CHAKWERA FOR BETTER WELFARE OF TRADITIONAL LEADERS

MBC Online

Malawi set to host ANOCA Zone VI Elective AGM

Yamikani Simutowe

Chakwera describes President Murmu’s visit as inspirational for girls

Beatrice Mwape
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.