Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News

Immigration iyamba kusindikiza ma Passport mawa

Ntchito yosindikiza ma Passport tsopano iyambanso mawa lachitatu ku Blantyre, Nthambi yoona zolowa ndikutuluka m’dziko muno, ya Immigration, yatsimikiza zimenezi.

Mneneri wa nthambiyi, a Wellington Chiponde, ati anthu onse ofuna ziphaso zoyendera, tsopano atha kuyamba kupita ku likulu la nthambiyi ku Blantyre kukapeza ziphasozi kuyambira tsikuli.

A Chiponde athokoza anthu m’dziko muno kamba kopilira pa nthawi imene nthambiyi imakonza zinthu kuti ziyambenso kuyenda bwino.

Anthu ofuna ziphaso akhala akumakatenga ziphasozi ku Lilongwe a Immigration atasiya kusindikiza ku Blantyre atathetsa mgwirizano ndi kampani yomwe inkapanga ziphasozi mmbuyomu.

 

Related posts

New solar initiative to boost MSMEs and drive economic growth

McDonald Chiwayula

‘Her Power Net initiative key to transforming the youth’

Rabson Kondowe

Defence wants Mary Bushiri discharged from extradition case

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.