Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News

Immigration iyamba kusindikiza ma Passport mawa

Ntchito yosindikiza ma Passport tsopano iyambanso mawa lachitatu ku Blantyre, Nthambi yoona zolowa ndikutuluka m’dziko muno, ya Immigration, yatsimikiza zimenezi.

Mneneri wa nthambiyi, a Wellington Chiponde, ati anthu onse ofuna ziphaso zoyendera, tsopano atha kuyamba kupita ku likulu la nthambiyi ku Blantyre kukapeza ziphasozi kuyambira tsikuli.

A Chiponde athokoza anthu m’dziko muno kamba kopilira pa nthawi imene nthambiyi imakonza zinthu kuti ziyambenso kuyenda bwino.

Anthu ofuna ziphaso akhala akumakatenga ziphasozi ku Lilongwe a Immigration atasiya kusindikiza ku Blantyre atathetsa mgwirizano ndi kampani yomwe inkapanga ziphasozi mmbuyomu.

 

Related posts

National Swimming Championship kicks off in Blantyre

Rabson Kondowe

STEPHANOS FOUNDATION SCALES OUT TO CENTRAL REGION OF MALAWI

McDonald Chiwayula

Boma la Neno lichita bwino polimbana ndi Edzi

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.