Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

FDH Bank yathandiza NFRA ndi chimanga

FDH Bank yapeleka chimanga chokwana matani 100 ku bungwe la National Food Reserve Agency (NFRA).

Mkulu wa zamalonda ku Banki ya FDH, a Levie Nkunika, wati achita izi potsatira pempho la mtsogoleri wa dziko lino loti dziko lino lili pa ngozi yanjala.

M’mawu ake, mkulu wa bungwe la NFRA, a George Macheka, wati ndikofunika kugwiranamanja pa ntchito yothandiza mabanja amene akhudzidwa ndi njala m’dziko muno.

Malinga ndi NFRA, dziko lino likufunika pafupifupi ma tani 200,000 kuti lithane ndi vuto lanjara.

Related posts

Immigration ikufuna kukhala ya mphamvu pa masewero

Rabson Kondowe

“Tisanaloze zala adindo tidziunike kaye ifeyo”

Romeo Umali

Apereka njinga zamoto zothandizira ntchito zaumoyo

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.