Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Asanu agwidwa ataba zipangizo zomangira bwalo la timu ya Wanderers

Apolisi ku Soche mu mzinda wa Blantyre amanga alonda awiri a kampani ya zomangamanga ya AFECC komanso anthu atatu ochita malonda pa sitolo ya hardware powaganizira kuti anaba katundu womangira bwalo la masewero la timu ya Mighty Mukuru Wanderers wa ndalama zokwana K10 million. 

Malinga ndi a Aaron Chilala amene ndi ofalitsankhani pa polisi ya Soche, anthuwa analongedza katunduyo mu galimoto koma apolisi anawagwira pamene amafuna adzituluka pamalopo.

Anthuwa: Nedson Pondani, 66 ndi Patrick Lime, 40 omwe ndi alonda komanso Weston Manyong’onya, 42, Henry Chanza, 41 ndi Rodgers Malembo, 42 omwe amachita malonda a hardware, ali mu chitokosi ndipo akuyembekezeka kukaonekera ku bwalo la milandu komwe akayankhe mlandu okuba.

 

Olemba : Charles Pensulo

Related posts

Blantyre District Hospital continues to get more support

Romeo Umali

NICE drills volunteers ahead of 2025 elections

Romeo Umali

Nsanje identifies 2024-2025 GESD, DDF projects contractors

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.