Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Anayi ali m’chitokosi ataba mowa wa K2.3 million

Apolisi m’boma la Mangochi amanga anthu anayi amene akuwaganizira kuti anathyola ndi kuba zakumwa zaukali zandalama pafupifupi K2.3 million pa malo ena ogulitsira mowa otchedwa ‘Pa Soko’.

Ofalitsankhani pa Polisi ya Mangochi, a Amina Tepani Daudi, anati mowa wina obedwa wapezeka ndipo mabotolo ena apezeka opanda kanthu.

“Mwini wake wa malowa anatidziwitsa kuti usiku wapa 8 September anatseka malowo cha m’ma 1 koloko m’mawa, koma kunja kutayera anazindikira kuti malowo anathyoledwa ndi anthu aupandu komanso anaba ndalama zokwana K120,000,” a Daudi anatero.

Anthu amene akuwaganizirawa ndi a Bongani Kachingwe, 26, Vincent Makhiringa, 32, Maxwell Shafi, 20 komanso Mkwanda Shahid, 22 ndipo akaonekera kubwalo lamilandu kuti akayankhe mulandu otchola nyumba ndi kuba katundu.

 

Related posts

Nkhondo ya mphunzitsi ndi ophunzira wake

Romeo Umali

‘Masewero ndi njira yofalitsa uthenga wa uchembere wabwino’

Romeo Umali

Human rights expert urges renewed approach to uphold right to food

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.